Langwan Piksy - Mthunzi lyrics | LyricsFreak
Correct  |  Mail  |  Print  |  Vote

Mthunzi Lyrics

Langwan Piksy – Mthunzi Lyrics

CHORUS
Ndikufuna mthunziwo
Sindufuna Nkhunizo
Chonde musadule
Mtengo wangawo

Nthawi zina sitikamba zofunika kukambidwa
Sitikankha zofunika kukankhidwa
Pena Sitikanda pofunika kukandidwa
Dziko linasintha timaopa kutayidwa

Ma born again
Sangacheze nawe unless you born again
But then again
Ndingasinthe bwanji ngati muku leader life ngati muli kumwamba kale
U seem so far away

Yesu anadzera ochimwa
Miyala yokanidwayo
These days ndiimene ikusalidwayo
Think again
If you really born again
Njira yanuyo tilondolereni

CHORUS
Ndikufuna mthunziwo
Sindufuna Nkhunizo
Chonde musadule
Mtengo wangawo

Abambo prophet akazi awo prophetess
Chondidabwitsa amakhala ndi confidence
Ine I thought zimayendera maitanidwe
Mesa ndimphatso
Yoti ena alibe

Pa banja panu mwayambisa yanu church
Dzina lake pa Google mwachita search
Tilibe mphavu zokupangirani judge
Koma ngati nku jahena chonde msatipange drag

Kuuza anthu amu mpingo mwanu alemera
Akhristu anu kupusa amayamba kusekelera
Amen!
Mulungu achita kothekera
Kusiya kulimbikira ntchito nkumangopemphera
Kenako amayamba nsanje
Mwawasocheretsa
Kukhulupira ulosi wanu mwawasokoneza
Awa nga satanic
Awa kukhwima chabe awa
Neba wachikunja walemera mtima ukuwawa

CHORUS
Ndikufuna mthunziwo
Sindufuna Nkhunizo
Chonde musadule
Mtengo wangawo

Mutiuze za kumwamba
Osati kumangotikomedwetsa nzapadziko pano
Pano

Muzinthu zonse, zonse zonse
Ambuye akhalemo
Amatero malembo
Upindulanji ndi za mdziko ukutaya moyo wako?

Musachulutse zokamba kuti tidzikuopani
Tidzikweza Mulungu osati tidzikupopani
Tidziona umulungu tikamakuonani
Sing along to the song

Muzinthu zonse, zonse, zonse
Muzinthu zonse Ambuye akhalemo

CHORUS
Ndikufuna mthunziwo
Sindufuna Nkhunizo
Chonde musadule
Mtengo wangawo
Share lyrics
×

Mthunzi comments