Langwan Piksy - Kuzizira lyrics | LyricsFreak
Correct  |  Mail  |  Print  |  Vote

Kuzizira Lyrics

Langwan Piksy – Kuzizira Lyrics

Kukumazizira kukada
Tsiku kuchedwa kutha kukacha
Tsiku lonse mvula mawawa
Sindingachedwe ndidziwe za mawa
Mano anga anthu sawaona
Sikweni kweni kusekelera
Usiku zindivuta kugona
Ngati udzudzu ndimachezera
Moyo wathu dzana unkakoma
Kachikondi kutsekemera
Ubwino opanda mwina ‘pena koma
Kachikondi kulemelera

CHORUS
Alipo akukukonda?
Alipo akukuhoda?
Alipo akukugwira?
Ndikungoganizira eya
Alipo akukuwuza amakukonda kuposa ine? ey
Poti dziko langa likuzizira popanda iwe yeah

VERSE TWO
Chikondi chinali on point
Ngati nyimbo yolondola ma note
Chinali perfect chinalibe fault
Anthu wokamba ankati tiri hot
Zoti chikondi chimawawa inali mphekesera
Anthu ena akamakamba tinkangomvetsera
Anthu akaduka kusowa chotigwetsera
Koma lero tandiona ndingo fwenthera
Maso anga ayandama in tears
Mtima wanga udzadza ndi fear
Usaganize zoti undisiye
Ndikungoganizira

CHORUS
Alipo akukukonda?
Alipo akukuhoda?
Alipo akukugwira?
Ndikungoganizira eya
Alipo akukuwuza amakukonda kuposa ine? ey
Poti dziko langa likuzizira popanda iwe yeah

VERSE THREE
Kodi chikondi nnakupatsa chija nchokwanira?
Kuti udzadikira mpaka nthawi idzakwanira?
Ngakhale moto utawotcha udzakakamira?
Chikondi chako chikuthawa kodi udzambwandira?
Ndiwe wekha ndikufuna mdziko langa dear
Mtima wako usakayike ndiwe wanga dziwa
Ndi pemphero langa nthawi zonse ukumbukira
Ndi kwa iwe kokha komwe mtima wanga ugundira

CHORUS
Alipo akukukonda?
Alipo akukuhoda?
Alipo akukugwira?
Ndikungoganizira eya
Alipo akukuwuza amakukonda kuposa ine? ey
Poti dziko langa likuzizira popanda iwe yeah
Share lyrics
×

Kuzizira comments